16. Potero aumphawi ali naco ciyembekezo,Ndi mphulupulu yatsekedwa pakamwa.
17. Taona, wodala munthu amene Mulungu amdzudzula;Cifukwa cace usapeputsa kulanga kwa Wamphamvuyonse.
18. Pakuti apweteka, namanganso mabala;Alasa, ndi manja ace omwe apoletsa.
19. Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi;Cinkana mwa asanu ndi awiri palibe coipa cidzakukhudza.
20. Adzakuombola kuimfa m'njala,Ndi ku mphamvu ya lupanga m'nkhondo.
21. Udzabisikira mkwapulo wa lilime,Sudzaciopanso cikadza cipasuko.