Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 5:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Potero aumphawi ali naco ciyembekezo,Ndi mphulupulu yatsekedwa pakamwa.

17. Taona, wodala munthu amene Mulungu amdzudzula;Cifukwa cace usapeputsa kulanga kwa Wamphamvuyonse.

18. Pakuti apweteka, namanganso mabala;Alasa, ndi manja ace omwe apoletsa.

19. Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi;Cinkana mwa asanu ndi awiri palibe coipa cidzakukhudza.

20. Adzakuombola kuimfa m'njala,Ndi ku mphamvu ya lupanga m'nkhondo.

21. Udzabisikira mkwapulo wa lilime,Sudzaciopanso cikadza cipasuko.

Werengani mutu wathunthu Yobu 5