Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 5:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Itana tsono; pali wina wakukuyankha kodi?Ndipo udzatembenukira kwa yani wa oyera mtimawo?

2. Pakuti mkwiyo umapha wopusa,Ndi nsanje imakantha wopanda pace.

3. Ndinapenya wopusa woyala mizu;Koma pomwepo ndinatemberera pokhala pace.

4. Ana ace akhala otekeseka, Napsinjika kucipata,Wopanda wina wakuwapulumutsa.

5. Zokolola zao anjala azidya,Azitenga ngakhale kuminga,Ndi aludzu ameza cuma cao.

6. Pakuti nsautso siituruka m'pfumbi,Ndi mabvuto saphuka m'nthaka;

7. Koma munthu abadwira mabvuto,Monga mbaliwali zikwera ziuluzika.

8. Koma ine ndikadafuna Mulungu,Ndikadaikira mlandu wanga Mulungu;

9. Amene acita zazikuru ndi zosalondoleka,Zinthu zodabwiza zosawerengeka.

10. Amene abvumbitsa mvula panthaka,Natumiza madzi paminda;

Werengani mutu wathunthu Yobu 5