Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 40:11-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tsanulira mkwiyo wako wosefuka,Nupenyerere ali yense wodzikuza ndi kumcepetsa,

12. Upenyerere ali yense wodzikuza, numtsitse,Nupondereze oipa pomwe akhala.

13. Uwakwirire pamodzi m'pfumbi,Uzimange nkhope zao pobisika.

14. Pamenepo inenso ndidzakubvomereza,Kuti dzanja lako lako lamanja likupulumutsa.

15. Tapenya tsono mvuu ndinaipanga pamodzi ndi iwe,Ikudya udzu ngati ng'ombe.

16. Tapenya tsono, mphamvu yace iri m'cuuno mwace,Ndi kulimbalimba kwace kuli m'mitsempha ya m'mimba yace.

17. Igwedeza mcira wace ngati mkungudza;Mitsempha ya ncafu zace ipotana.

18. Mafupa ace akunga misiwe yamkuwa;Ziwalo zace zikunga zitsulo zamphumphu,

19. Iyo ndiyo ciyambi ca macitidwe a Mulungu;Wakuilenga anaininkha lupanga lace.

20. Pakuti mapiri aiphukitsira cakudya,Kumene zisewera nyama zonse za kuthengo,

21. Igona pansi patsinde pa mitengo yamthunzi,Pobisala pabango ndi pathawale.

Werengani mutu wathunthu Yobu 40