1. Ndipo Yehova anabwereza kwa Yobu, nati,
2. Kodi wodzudzulayo atsutsane ndi Wamphamvuyonse?Wocita makani ndi Mulungu ayankhe.
3. Pamenepo Yobu anayankha Yehova, nati,
4. Taonani, ndakhululuka ine, ndidzakubwezerani mau otani?Ndigwira pakamwa.
5. Ndalankhula kamodzi, koma sindidzayankha;Inde kawiri, koma sindionjezanso.
6. Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,
7. Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndidzakufunsa, undidziwitse.