Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 4:12-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Anditengera mau m'tseri,M'khutu mwanga ndinalandira kunong'oneza kwace.

13. M'malingaliro a masomphenya a usiku,Powagwira anthu tulo tatikuru,

14. Anandidzera mantha ndi kunjenjemera,Nanthunthumira nako mafupa anga onse.

15. Pamenepo panapita mzimu pamaso panga;Tsitsi la thupi langa lidati nyau nyau.

16. Unaima ciriri, koma sindinatha kuzindikira maonekedwe ace;Panali mzukwa pamaso panga;Kunali cete, ndipo ndidamva mau akuti,

17. Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?

18. Taona, sakhulupirira atumiki ace;Nawanenera amithenga ace zopusa;

19. Kopambana kotani nanga iwo akukhala m'nyumba zadothi,Amene kuzika kwao kuti m'pfumbi,Angothudzulidwa ngati gulugufe,

20. Kuyambira m'mawa kufikira madzulo athudzuka;Aonongeka kosatha, osasamalirako munthu.

21. Kukometsetsa kwao sikumacotsedwa nao?Amafa koma opanda nzeru.

Werengani mutu wathunthu Yobu 4