Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 4:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2. Munthu akayesa kunena nawe mau, kodi udzamva nao cisoni?Koma akhoza ndani kudziletsa kunena?

3. Taona iwe walangiza aunyinji,Walimbitsa manja a ofoka.

4. Mau ako anacirikiza iye amene akadagwa,Walimbitsanso maondo otewa.

5. Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka;Cikukhudza, ndipo ubvutika.

6. Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu,Ndi ciyembekezo cako si ndiwo ungwiro wa njira zako?

7. Takumbukila tsopano, watayika ndani wosaparamula konse?Kapena oongoka mtima alikhidwa kuti?

Werengani mutu wathunthu Yobu 4