1. Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,
2. Munthu akayesa kunena nawe mau, kodi udzamva nao cisoni?Koma akhoza ndani kudziletsa kunena?
3. Taona iwe walangiza aunyinji,Walimbitsa manja a ofoka.
4. Mau ako anacirikiza iye amene akadagwa,Walimbitsanso maondo otewa.
5. Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka;Cikukhudza, ndipo ubvutika.