Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 39:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ana ao akhala ojinca, akulira kuthengo,Acoka osabwerera kwa amao.

5. Ndani walola mbidzi ituruke yaufulu?Anaimasulira mbidzi nsinga zace ndani,

6. Imene ndaciyesa cipululu nyumba yace,Ndi dziko lakhulo pokhala pace?

7. Aseka phokoso la kumudzi,Osamva kukuwa kwa wofulumiza nyama za m'goli.

8. Poyenda ponse pamapiri mpa busa pace;Ilondola caciwisi ciri conse.

9. Kodi njati idzabvomera kukutumikira,Idzakhala ku codyetseramo cako kodi?

10. Kodi ukhoza kumanga njati ndi lamba lace ilime m'mcera?Kapena idzakutsata kodi kufafaniza nthumbira m'zigwa?

11. Udzaikhulupirira kodi, popeza mphamvu yace njaikuru?Udzaisiyira nchito yako kodi?

Werengani mutu wathunthu Yobu 39