26. Kodi kabawi auluka mwa nzeru zako,Natambasula mapiko ace kumka kumwera?
27. Kodi ciombankhanga cikwera m'mwamba pocilamulira iwe,Nicimanga cisanja cace m'mwamba?
28. Kwao nku thanthwe, cigona komweko,Pansonga pa thanthwe pokhazikikapo.
29. Pokhala kumeneko ciyang'ana cakudya;Maso ace acipenyetsetsa ciri kutali,