Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 39:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ukhoza kodi kuwerenga miyezi yakuzipitira,Kapena udziwa nyengo yoti ziswane?

3. Zithuntha, ziswa,Zitaya zowawa zao.

4. Ana ao akhala ojinca, akulira kuthengo,Acoka osabwerera kwa amao.

5. Ndani walola mbidzi ituruke yaufulu?Anaimasulira mbidzi nsinga zace ndani,

6. Imene ndaciyesa cipululu nyumba yace,Ndi dziko lakhulo pokhala pace?

Werengani mutu wathunthu Yobu 39