Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 39:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Iumira mtima ana ace monga ngati sali ace;Idzilemetsa ndi nchito cabe, popeza iribe mantha;

17. Pakuti Mulungu anaimana nzeru,Ndipo sanaigawira luntha.

18. Ikafika nthawi yace, iweramuka,Iseka kavalo ndi wa pamsana pace.

19. Wampatsa kavalo mphamvu yace kodi?Wambveka pakhosi pace cenjerere cogwedezeka?

20. Wamlumphitsa kodi ngati dzombe?Ulemerero wa kumina kwace ngwoopsa.

21. Apalasa kucigwa, nakondwera nayo mphamvu yace;Aturuka kukomana nao eni zida.

Werengani mutu wathunthu Yobu 39