Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 38:34-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Kodi udziwa kukwezera mau ako kumitambo,Kuti madzi ocuruka akukute?

35. Kodi ukhoza kutumiza mphezi kuti zimuke,Ndi kunena nawe, Tiri pano?

36. Ndani analonga nzeru m'mitambomo?Ndani waninkha nyenyezi yotsotsoka luntha?

37. Adziwa ndani kuwerenga mitambo mwanzeru,Ndi kutsanulira micenje ya kuthambo ndani,

38. Pokandika pfumbi,Ndi kuundana zibuma pamodzi?

39. Kodi ukhoza kusakira mkango waukazi nyama?Ndi kukwaniritsa cakudya ca misona,

40. Pamene ibwathama m'ngaka mwao,Nikhala mobisala kulaliramo?

Werengani mutu wathunthu Yobu 38