Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 38:30-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Madzi aundana ngati mwala,Ndi pamwamba pa nyanja yozama mpogwirana madzi.

31. Kodi ungamange gulu la Nsangwe?Kapena kumasula zomangira za Akamwiniatsatana?

32. Ungaturutse kodi nyenyezi m'nyengo zao monga mwa malongosoledwe ao?Kapena kutsogolera Mlalang'amba ndi ana ace?

33. Kodi udziwa malemba a kuthambo?Ukhoza kukhazikitsa ufumu wao pa dziko lapansi?

34. Kodi udziwa kukwezera mau ako kumitambo,Kuti madzi ocuruka akukute?

35. Kodi ukhoza kutumiza mphezi kuti zimuke,Ndi kunena nawe, Tiri pano?

36. Ndani analonga nzeru m'mitambomo?Ndani waninkha nyenyezi yotsotsoka luntha?

Werengani mutu wathunthu Yobu 38