Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 38:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Njira iri kuti yomukira pogawikana kuunika,Kapena pomwazikira mphepo ya kum'mawa pa dziko lapansi?

25. Ndani anacikumbira mcera cimvula,Kapena njira ya bingu la mphezi,

26. Kubvumbitsa mvula pa dziko lapanda anthu,Ku cipululu kosakhala munthu,

27. Kukhutitsa thengo la kunkhwangwala,Ndi kuphukitsa msipu?

28. Kodi mvula iri naye atate?Kapena wabala ndani madontho amame?

Werengani mutu wathunthu Yobu 38