Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 38:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndi kuunika kwa oipa kuletsedwa kuti asakuone,Ndi dzanja losamulidwa lityoledwa.

16. Kodi unalowa magwero a nyanja?Kodi unayendayenda pozama peni peni?

17. Kodi zipata za imfa zinabvumbulukira iwe?Kapena kodi unaona zipata za mthunzi wa imfa?

18. Kodi unazindikira citando ca dziko lapansi?Fotokozera, ngati ucidziwa conse.

19. Iri kuti njira yomukira pokhala kuunika?Ndi mdima, pokhala pace pali kuti,

20. Kuti upite nao ku malire ace,Kuti uzindikire miseu ya ku nyumba yace?

21. Udziwa, pakuti unabadwa pamenepo,Ndi masiku ako acuruka kuwerenga kwao.

22. Kodi unalowa m'zosungiramo cipale cofewa?Kapena unapenya zosungiramo matalala,

23. Amene ndiwasungira tsiku la nsautso,Tsiku lakulimbana nkhondo?

24. Njira iri kuti yomukira pogawikana kuunika,Kapena pomwazikira mphepo ya kum'mawa pa dziko lapansi?

25. Ndani anacikumbira mcera cimvula,Kapena njira ya bingu la mphezi,

26. Kubvumbitsa mvula pa dziko lapanda anthu,Ku cipululu kosakhala munthu,

27. Kukhutitsa thengo la kunkhwangwala,Ndi kuphukitsa msipu?

Werengani mutu wathunthu Yobu 38