Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 38:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Yehova anayankha Yobu m'kabvumvulu, nati,

2. Ndani uyu adetsa uphungu,Ndi mau opanda nzeru?

3. Udzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndikufunsa, undidziwitse.

4. Unali kuti muja ndinaika maziko a dziko lapansi?Fotokoza ngati udziwa kuzindikira.

5. Analemba malire ace ndani, papeza udziwa?Anayesapo cingwe cace ndani?

6. Maziko ace anakumbidwa pa ciani?Kapena anaika ndani mwala wace wa pangondya,

7. Muja nyenyezi za m'mawa zinayimba limodzi mokondwera,Ndi ana onse a Mulungu anapfuula ndi cimwemwe?

8. Kapena anatseka nyanja ndani ndi zitseko,Muja idakamula ngati kuturuka m'mimba,

9. Muja ndinayesa mtambo cobvala cace,Ndi mdima wa bii nsaru yace yakulunga,

Werengani mutu wathunthu Yobu 38