1. Pamenepo Yehova anayankha Yobu m'kabvumvulu, nati,
2. Ndani uyu adetsa uphungu,Ndi mau opanda nzeru?
3. Udzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndikufunsa, undidziwitse.
4. Unali kuti muja ndinaika maziko a dziko lapansi?Fotokoza ngati udziwa kuzindikira.
5. Analemba malire ace ndani, papeza udziwa?Anayesapo cingwe cace ndani?
6. Maziko ace anakumbidwa pa ciani?Kapena anaika ndani mwala wace wa pangondya,