Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 37:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Mutilangize cimene tidzanena ndi Iye;Sitidziwa kulongosola mau athu cifukwa ca mdima.

20. Kodi munthu ayenera kumuuza kuti ndifuna kunena,Kapena kodi munthu adzakhumba kumezedwa?

21. Ndipo tsopano anthu sakhoza kupenyerera kuunika pakunyezimira kuthambo,Ndi mphepo yapita ndi kuuyeretsa,

22. Kucokera kumpoto kudzera kuwala konyezimira,Mulungu ali nao ukulu woopsa.

23. Kunena za Wamphamvuyonse, sitingamsanthule; ndiye wa mphamvu yoposa;Koma mwa ciweruzo ndi cilungamo cocuruka samasautsa.

24. M'mwemo anthu amuopa,Iye sasamalira ali yense wanzeru mumtima.

Werengani mutu wathunthu Yobu 37