Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 37:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ngati aufikitsira dziko lace kulidzudzula,Kapena kulicitira cifundo.

14. Tamverani ici, Yobu.Taimani, mulingirire zodabwiza za Mulungu.

15. Kodi mudziwa umo Mulungu azilangizira zimenezi,Nawalitsa mphezi ya m'mtambo mwace?

16. Kodi mudziwa madendekeredwe ace a mitambo,Zodabwiza za Iye wakudziwa mwangwiro?

17. Kodi mudziwa umo zobvala zanu zifundira,Pamene dziko liri thuu cifukwa ca mwela?

18. Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye,Ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?

19. Mutilangize cimene tidzanena ndi Iye;Sitidziwa kulongosola mau athu cifukwa ca mdima.

20. Kodi munthu ayenera kumuuza kuti ndifuna kunena,Kapena kodi munthu adzakhumba kumezedwa?

21. Ndipo tsopano anthu sakhoza kupenyerera kuunika pakunyezimira kuthambo,Ndi mphepo yapita ndi kuuyeretsa,

Werengani mutu wathunthu Yobu 37