Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 37:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pa icinso mtima wanga unienjemera,Nusunthika m'malo mwace.

2. Mvetsetsani cibumo ca mau ace,Ndi kugunda koturuka m'kamwa mwace.

3. Akumveketsa pansi pa thambo ponse,Nang'anipitsa mphezi yace ku malekezero a dziko lapansi.

4. Mau abuma kuitsata,Agunda ndi mau a ukulu wace,Ndipo sailetsa atamveka mau ace,

5. Mulungu agunda modabwitsa ndi mau ace,Acita zazikuru osazidziwa ife.

Werengani mutu wathunthu Yobu 37