Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 36:8-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo akamangidwa m'nsinga,Nakakodwa ndi zingwe za mazunzo,

9. Pamenepo awafotokozera nchito zao,Ndi zolakwa zao, kuti anacita modzikuza.

10. Awatseguliranso m'khutu mwao kuti awalangize,Nawauza abwerere kuleka mphulupulu.

11. Akamvera ndi kumtumikira,Adzatsiriza masiku ao modala,Ndi zaka zao mokondwera.

12. Koma akapanda kumvera adzatayika ndi lupanga,Nadzatsirizika osadziwa kanthu.

13. Koma iwo a mtima wakunyoza Mulungu, akundika mkwiyo,Akawamanga Iye, sapfuulira.

14. Iwowa akufa akali biriwiri,Ndi moyo wao utayika ngati odetsedwa.

15. Apulumutsa wozunzika mwa kuzunzika kwace,Nawatsegulira m'khutu mwao mwa kupsinjika kwao.

16. Inde akadakukopani mucoke posaukira,Mulowe kucitando kopanda copsinja;Ndipo zoikidwa pagome panu zikadakhala zonona ndithu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 36