Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 36:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndidzatenga nzeru zanga kutali,Ndidzabvomereza kuti Mlengi wanga ndi wolungama.

4. Pakuti zoonadi, mau anga sali abodza,Wakudziwitsa mwangwiro ali nanu.

5. Taonani, Mulungu ndiye mwini mphamvu, ndipo sapeputsa munthu;Mphamvu ya nzeru zace ndi yaikuru.

6. Sasunga woipa akhale ndi moyo,Koma awaninkha ozunzikazowayenera iwo.

7. Sawacotsera wolungama maso ace,Koma pamodzi ndi mafumu pa mpando waoAwakhazika cikhazikire, ndipo akwezeka.

8. Ndipo akamangidwa m'nsinga,Nakakodwa ndi zingwe za mazunzo,

9. Pamenepo awafotokozera nchito zao,Ndi zolakwa zao, kuti anacita modzikuza.

10. Awatseguliranso m'khutu mwao kuti awalangize,Nawauza abwerere kuleka mphulupulu.

11. Akamvera ndi kumtumikira,Adzatsiriza masiku ao modala,Ndi zaka zao mokondwera.

12. Koma akapanda kumvera adzatayika ndi lupanga,Nadzatsirizika osadziwa kanthu.

13. Koma iwo a mtima wakunyoza Mulungu, akundika mkwiyo,Akawamanga Iye, sapfuulira.

14. Iwowa akufa akali biriwiri,Ndi moyo wao utayika ngati odetsedwa.

15. Apulumutsa wozunzika mwa kuzunzika kwace,Nawatsegulira m'khutu mwao mwa kupsinjika kwao.

16. Inde akadakukopani mucoke posaukira,Mulowe kucitando kopanda copsinja;Ndipo zoikidwa pagome panu zikadakhala zonona ndithu.

17. Koma mukadzazidwa nazo zolingirira oipa,Zolingirirazo ndi ciweruzo zidzakugwiranibe,

Werengani mutu wathunthu Yobu 36