Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 36:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Koma mukadzazidwa nazo zolingirira oipa,Zolingirirazo ndi ciweruzo zidzakugwiranibe,

18. Pakuti mucenjere, mkwiyo ungakunyengeni mucite mnyozo;Ndipo usakusokeretseni ukulu wa dipoli.

19. Cuma canu cidzafikira kodi, kuti simudzakhala wopsinjika,Kapena mphamvu yanu yonse yolimba?

20. Musakhumbe usiku,Umene anthu alikhidwe m'malo mwao.

21. Cenjerani, musaluniike kumphulupulu;Pakuti mwaisankha iyi mutazunzidwa.

22. Taonani, Mulungu acita mokwezeka mu mphamvu yace,Mphunzitsi wakunga Iye ndani?

Werengani mutu wathunthu Yobu 36