Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:9-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti anati, Munthu sapindula kanthu nakoKubvomerezana naye Mulu ngu.

10. Cifukwa cace mundimvere ine, eni nzeru inu,Nkutali ndi Mulungu kucita coipa,Ndi Wamphamvuyonse kucita cosalungama.

11. Pakuti ambwezera munthu monga mwa nchito yace,Napezetsa munthu ali yense monga mwa mayendedwe ace.

12. Ndithu zoonadi, Mulungu sangacite coipa,Ndi Wamphamvuyonse sangaipse mlandu.

13. Anamuikiza dziko lapansi ndani?Kapena anakonzeratu dziko lonse lokhalamo anthu ndani?

14. Akadzikumbukila yekha mumtima mwace,Akadzisonkhanitsira yekha mzimu wace ndi mpweya wace,

15. Zamoyo zonse zidzatsirizika pamodzi,Ndi munthu adzabwerera kupfumbi.

16. Ngati tsono uli nako kuzindikira, tamvera ici,Cherera khutu kunena kwanga.

17. Kodi munthu woipidwa naco ciweruzo adzalamulira?Ndipo kodi utsutsa wolungama ndi wamphamvuyo kuti ngwoipa?

18. Kodi kuyenera kunena kwa mfumu, Wopanda pace iwe,Kapena kwa akalonga, Oipa inu?

19. Nanga kwa Iye wosasamalira nkhope za akalonga,Wosasiyanitsa pakati pa wolemera ndi wosauka?Pakuti onsewo ndiwo nchito ya manja ace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 34