Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:28-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. M'mwemo anafikitsa kwa Iye kupfuula kwa osauka;Ndipo anamva Iye kupfuula kwa ozunzika.

29. Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani?Akabisa nkhope yace adzampenyerera ndani?Cikacitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, ncimodzimodzi;

30. Kuti munthu wonyoza Mulungu asacite ufumu,Ndi anthu asakodwe mumsampha,

31. Pakuti pali wina kodi anati kwa Mulungu,Ndasenza kulanga kwanu, ndingakhale sindinalakwa?

32. Cimene sindiciona mundilangize ndi Inu,Ngati ndacita cosalungama sindidzabwerezanso.

33. Kodi cilango ca Mulungu cikhale monga mucifuna inu, pakuti mucikana?Musankhe ndi inu, ine ai;M'mwemo monga mudziwa, nenani.

34. Anthu ozindikira adzanena nane,Inde anthu anzeru onse akundimva adzati,

35. Yobu alankhula wopanda kudziwa,Ndi mau ace alibe nzeru.

36. Mwenzi nayesedwe Yobu kufikira kutha,Cifukwa ca kuyankha kwace monga anthu amphulupulu,

Werengani mutu wathunthu Yobu 34