Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:22-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Palibe mdima kapena mthunzi wa imfa,Kuti ocita zopanda pace abisaleko.

23. Pakuti Mulungu alibe cifukwa ca kulingiriranso za munthu,Kuti afike kwa. Iye kudzaweruzidwa.

24. Aphwanya eni mphamvu osaturutsa kubwalo mlandu wao,Naika ena m'malo mwao.

25. Pakuti asamalira nchito zao,Nawagubuduza usiku kuti aphwanyike.

26. Awakantha ngati oipa,Poyera pamaso pa anthu.

27. Popeza anapambuka, naleka kumtsata,Osasamalira njira zace ziri zonse.

28. M'mwemo anafikitsa kwa Iye kupfuula kwa osauka;Ndipo anamva Iye kupfuula kwa ozunzika.

29. Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani?Akabisa nkhope yace adzampenyerera ndani?Cikacitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, ncimodzimodzi;

30. Kuti munthu wonyoza Mulungu asacite ufumu,Ndi anthu asakodwe mumsampha,

31. Pakuti pali wina kodi anati kwa Mulungu,Ndasenza kulanga kwanu, ndingakhale sindinalakwa?

32. Cimene sindiciona mundilangize ndi Inu,Ngati ndacita cosalungama sindidzabwerezanso.

33. Kodi cilango ca Mulungu cikhale monga mucifuna inu, pakuti mucikana?Musankhe ndi inu, ine ai;M'mwemo monga mudziwa, nenani.

34. Anthu ozindikira adzanena nane,Inde anthu anzeru onse akundimva adzati,

35. Yobu alankhula wopanda kudziwa,Ndi mau ace alibe nzeru.

Werengani mutu wathunthu Yobu 34