Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:19-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Nanga kwa Iye wosasamalira nkhope za akalonga,Wosasiyanitsa pakati pa wolemera ndi wosauka?Pakuti onsewo ndiwo nchito ya manja ace.

20. M'kamphindi akufa, ngakhale pakati pa usiku,Anthu agwedezeka, napita,Amphamvu acotsedwa opanda dzanja lakuwacotsa.

21. Pakuti maso ace ali pa njira ya munthu ali yense,Napenya moponda mwace monse.

22. Palibe mdima kapena mthunzi wa imfa,Kuti ocita zopanda pace abisaleko.

23. Pakuti Mulungu alibe cifukwa ca kulingiriranso za munthu,Kuti afike kwa. Iye kudzaweruzidwa.

24. Aphwanya eni mphamvu osaturutsa kubwalo mlandu wao,Naika ena m'malo mwao.

25. Pakuti asamalira nchito zao,Nawagubuduza usiku kuti aphwanyike.

26. Awakantha ngati oipa,Poyera pamaso pa anthu.

27. Popeza anapambuka, naleka kumtsata,Osasamalira njira zace ziri zonse.

28. M'mwemo anafikitsa kwa Iye kupfuula kwa osauka;Ndipo anamva Iye kupfuula kwa ozunzika.

29. Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani?Akabisa nkhope yace adzampenyerera ndani?Cikacitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, ncimodzimodzi;

Werengani mutu wathunthu Yobu 34