Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:17-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kodi munthu woipidwa naco ciweruzo adzalamulira?Ndipo kodi utsutsa wolungama ndi wamphamvuyo kuti ngwoipa?

18. Kodi kuyenera kunena kwa mfumu, Wopanda pace iwe,Kapena kwa akalonga, Oipa inu?

19. Nanga kwa Iye wosasamalira nkhope za akalonga,Wosasiyanitsa pakati pa wolemera ndi wosauka?Pakuti onsewo ndiwo nchito ya manja ace.

20. M'kamphindi akufa, ngakhale pakati pa usiku,Anthu agwedezeka, napita,Amphamvu acotsedwa opanda dzanja lakuwacotsa.

21. Pakuti maso ace ali pa njira ya munthu ali yense,Napenya moponda mwace monse.

22. Palibe mdima kapena mthunzi wa imfa,Kuti ocita zopanda pace abisaleko.

23. Pakuti Mulungu alibe cifukwa ca kulingiriranso za munthu,Kuti afike kwa. Iye kudzaweruzidwa.

24. Aphwanya eni mphamvu osaturutsa kubwalo mlandu wao,Naika ena m'malo mwao.

25. Pakuti asamalira nchito zao,Nawagubuduza usiku kuti aphwanyike.

Werengani mutu wathunthu Yobu 34