Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 34:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti ambwezera munthu monga mwa nchito yace,Napezetsa munthu ali yense monga mwa mayendedwe ace.

12. Ndithu zoonadi, Mulungu sangacite coipa,Ndi Wamphamvuyonse sangaipse mlandu.

13. Anamuikiza dziko lapansi ndani?Kapena anakonzeratu dziko lonse lokhalamo anthu ndani?

14. Akadzikumbukila yekha mumtima mwace,Akadzisonkhanitsira yekha mzimu wace ndi mpweya wace,

15. Zamoyo zonse zidzatsirizika pamodzi,Ndi munthu adzabwerera kupfumbi.

Werengani mutu wathunthu Yobu 34