8. Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,
9. Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.
10. Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;
11. Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.
12. Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.
13. Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji?Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.
14. Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.
15. M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,
16. Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;
17. Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;