Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 33:14-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.

15. M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,

16. Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;

17. Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;

18. Kuti amletse angaonongeke,Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.

19. Alangidwanso ndi zowawa pakama pace,Ndi kulimbana kowawa kosapuma m'mafupa ace.

20. M'mwemo mtima wace ucita mseru ndi mkate,Ndi moyo wace pa cakudya colongosoka.

21. Mnofu wace udatha, kuti sungapenyeke;Ndi mafupa ace akusaoneka aturuka.

22. Inde wasendera kufupi ku manda,Ndi moyo wace kwa akuononga.

23. Akakhala kwa iye mthenga,Womasulira mau mmodzi mwa cikwi,Kuonetsera munthu comuyenera;

24. Pamenepo Mulungu amcitira cifundo, nati,Mlanditse, angatsikire kumanda,Ndampezera dipo.

25. Mnofu wace udzakhala se, woposa wa mwana;Adzabwerera ku masiku a ubwana wace.

26. Apembedza Mulungu, ndipo amkomera mtima;M'mwemo aona nkhope yace mokondwera;Ndipo ambwezera munthu cilungamo cace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 33