Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 33:10-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;

11. Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.

12. Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.

13. Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji?Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.

14. Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.

15. M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,

16. Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;

17. Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;

18. Kuti amletse angaonongeke,Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.

19. Alangidwanso ndi zowawa pakama pace,Ndi kulimbana kowawa kosapuma m'mafupa ace.

20. M'mwemo mtima wace ucita mseru ndi mkate,Ndi moyo wace pa cakudya colongosoka.

21. Mnofu wace udatha, kuti sungapenyeke;Ndi mafupa ace akusaoneka aturuka.

22. Inde wasendera kufupi ku manda,Ndi moyo wace kwa akuononga.

23. Akakhala kwa iye mthenga,Womasulira mau mmodzi mwa cikwi,Kuonetsera munthu comuyenera;

24. Pamenepo Mulungu amcitira cifundo, nati,Mlanditse, angatsikire kumanda,Ndampezera dipo.

25. Mnofu wace udzakhala se, woposa wa mwana;Adzabwerera ku masiku a ubwana wace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 33