Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 33:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Komatu, Yobu, mumvere maneno anga,Mucherere khutu mau anga.

2. Taonani tsono, ndatsegula pakamwa panga,Lilime langa lanena m'kamwa mwanga.

3. Maneno anga aulula ciongoko ca mtima wanga,Ndi monga umo idziwira milomo yanga idzanena zoona.

4. Mzimu wa Mulungu unandilenga,Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse umandipatsa moyo.

5. Ngati mukhoza, mundiyankhe;Mulongosolere mau anu pamaso panga, mukonzeke.

6. Taonani, ndikhala kwa Mulungu ngati inu;Inenso ndinaumbidwa ndi dothi,

7. Taonani, kuopsa kwanga simudzacita nako mantha;Ndi ici ndikusenzetsani sicidzakulemererani.

8. Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,

Werengani mutu wathunthu Yobu 33