Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 32:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Akulu sindiwo eni nzeru,Ndi okalamba sindiwo ozindikira ciweruzo.

10. Cifukwa cace ndinati, Ndimvereni ine,Inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.

11. Taonani, ndinalindira mau anu,Ndinacherera khutu zifukwa zanu,Pofunafuna inu ponena.

12. Inde ndinasamalira inu;Koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu,Kapena wakumbwezera mau pakati painu.

13. Msamati, Tapeza nzeru ndife,Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;

14. Popeza sanandiponyera ine mau,Sindidzamyankha ndi maneno anu.

15. Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.

16. Kodi ndidzangolindira popeza sanena iwo,Popeza akhala du osayankhanso?

17. Ndidzayankha inenso mau anga,Ndidzaonetsa inenso za m'mtima mwanga.

Werengani mutu wathunthu Yobu 32