Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 32:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Msamati, Tapeza nzeru ndife,Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;

14. Popeza sanandiponyera ine mau,Sindidzamyankha ndi maneno anu.

15. Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.

16. Kodi ndidzangolindira popeza sanena iwo,Popeza akhala du osayankhanso?

17. Ndidzayankha inenso mau anga,Ndidzaonetsa inenso za m'mtima mwanga.

18. Pakuti ndadzazidwa ndi mau,Ndi mzimu wa m'kati mwanga undifulumiza.

19. Taonani, m'cifuwa mwanga muli ngati vinyo wosowa popungulira,Ngati matumba atsopano akuti aphulike.

20. Ndidzanena kuti cifundo citsike;Ndidzatsegula milomo yanga ndi kuyankha.

21. Ndisati ndisamalire nkhope ya munthu,Kapena kumchula munthu maina omdyola nao;

Werengani mutu wathunthu Yobu 32