1. Pamenepo amuna atatuwa analeka kumyankha Yobu; pakuti anali wolungama pamaso pace pa iye mwini.
2. Ndipo adapsa mtima Elihu mwana wa Barakeli wa ku Buzi, wa cibale ca Ramu, adapsa mtima pa Yobu; pakuti anadziyesera yekha wolungama, wosati Mulungu.
3. Adapsa mtima pa mabwenzi ace atatu omwe, pakuti anasowa pomyankha; koma anamtsutsa Yobu kuti ali woipa.