28. Icinso ndi mphulupulu yoyenera oweruza kunena mlandu wace;Pakuti ndikadakana Mulungu ali m'mwamba.
29. Ngati ndakondwera nalo tsoka la wondida,Kapena kudzitukula pompeza coipa;
30. Ndithu sindinalola m'kamwa mwanga mucimwe,Kupempha motemberera moyo wace.
31. Ngati amuna a m'hema mwanga sanati,Ndani adzapeza munthu wosakhuta nyama yomgawira Yobu?
32. Mlendo sakagona pakhwalala,Koma ndinatsegulira wam'njira pakhomo panga.
33. Ngati ndakwirira zolakwa zanga monga Adamu,Ndi kubisa mphulupulu yanga m'cifuwa mwanga;