Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 31:23-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

24. Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga,Ndi kunena ndi golidi woyengetsa,Ndiwe cikhazikitso canga;

25. Ngati ndinakondwera popeza cuma canga ncacikuru,Ndi dzanja langa lapeza zocuruka;

26. Ngati ndalambira dzuwa lirikuwala,Kapena mwezi ulikuyenda monyezimira;

27. Ndi mtima wanga wakopeka m'tseri,Ndi pakamwa panga padapsompsona dzanja langa;

28. Icinso ndi mphulupulu yoyenera oweruza kunena mlandu wace;Pakuti ndikadakana Mulungu ali m'mwamba.

29. Ngati ndakondwera nalo tsoka la wondida,Kapena kudzitukula pompeza coipa;

30. Ndithu sindinalola m'kamwa mwanga mucimwe,Kupempha motemberera moyo wace.

31. Ngati amuna a m'hema mwanga sanati,Ndani adzapeza munthu wosakhuta nyama yomgawira Yobu?

32. Mlendo sakagona pakhwalala,Koma ndinatsegulira wam'njira pakhomo panga.

33. Ngati ndakwirira zolakwa zanga monga Adamu,Ndi kubisa mphulupulu yanga m'cifuwa mwanga;

34. Popeza ndinaopa unyinji waukuru,Ndi cipepulo ca mapfuko cinandiopsetsa;Potero ndinakhala cete osaturuka pakhomo panga.

35. Ha! ndikadakhala naye wina wakundimvera,Cizindikilo canga sici, Wamphamvuyonse andiyankhe;Mwenzi ntakhala nao mau akundineneza analemberawo mdani wangal

36. Ndithu ndikadawasenza paphewa panga,Ndi kudzimangirira awa ngati korona.

37. Ndikadamfotokozera ciwerengo ca mopondamo mwanga,Ndikadamsenderera Iye ngati ka longa,

38. Ngati minda yanga ipfuula monditsutsa,Ndi nthumbira zace zilira pamodzi;

Werengani mutu wathunthu Yobu 31