Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 31:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa,Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;

22. Libanthuke phewa langa paphalo,Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.

23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

24. Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga,Ndi kunena ndi golidi woyengetsa,Ndiwe cikhazikitso canga;

25. Ngati ndinakondwera popeza cuma canga ncacikuru,Ndi dzanja langa lapeza zocuruka;

Werengani mutu wathunthu Yobu 31