2. Pakuti gawo la Mulungu locokera kumwamba,Ndi colowa ca Wamphamvuyonse cocokera m'mwambamo nciani?
3. Si ndizo cionongeko ca wosalungama,Ndi tsoka la ocita mphulupulu?
4. Nanga sapenyanjira zanga,Ndi kuwerenga moponda mwanga monse?
5. Ngati ndinayanjana nalo bodza,Ndi phazi langa linathamangira cinyengo;
6. Andiyese ndi muyeso wolingana,Kuti Mulungu adziwe ungwiro wanga.