Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 31:14-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndidzatani ponyamuka Mulungu?Ndipo pondizonda Iye ndidzamyankha ciani?

15. Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenga iyenso?Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?

16. Ngati ndakaniza aumphawi cifuniro cao,Kapena kutopetsa maso a amasiye,

17. Kapena kudya nthongo yanga ndekha,Osadyako mwana wamasiye;

18. (Pakuti kuyambira ubwana wanga analeredwa ndi ine monga ndi atate;Ndipo ndinakhala nkhoswe ya wamasiye cibadwire ine.)

19. Ngati ndinaona wina alinkutayika wopanda cobvala,Kapena kuti wosowa alibe copfunda;

20. Ngati zuuno zace sizinandiyamika,Ngati sanapfunda ubweya wa nkhosa zanga;

21. Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa,Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;

22. Libanthuke phewa langa paphalo,Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.

23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

24. Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga,Ndi kunena ndi golidi woyengetsa,Ndiwe cikhazikitso canga;

Werengani mutu wathunthu Yobu 31