Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 31:10-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mkazi wanga aperere wina;Wina namuike kumbuyo.

11. Pakuti ico ndi coipitsitsa,Ndico mphulupulu yoyenera oweruza anene mlandu wace.

12. Pakuti ndico moto wakunyeka mpaka cionongeko,Ndi cakuzula zipatso zanga zonse.

13. Ngati ndapeputsa mlandu wa kapolo wanga, kapena wa mdzakazi wanga,Potsutsana nane iwo,

14. Ndidzatani ponyamuka Mulungu?Ndipo pondizonda Iye ndidzamyankha ciani?

15. Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenga iyenso?Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?

16. Ngati ndakaniza aumphawi cifuniro cao,Kapena kutopetsa maso a amasiye,

17. Kapena kudya nthongo yanga ndekha,Osadyako mwana wamasiye;

18. (Pakuti kuyambira ubwana wanga analeredwa ndi ine monga ndi atate;Ndipo ndinakhala nkhoswe ya wamasiye cibadwire ine.)

19. Ngati ndinaona wina alinkutayika wopanda cobvala,Kapena kuti wosowa alibe copfunda;

20. Ngati zuuno zace sizinandiyamika,Ngati sanapfunda ubweya wa nkhosa zanga;

21. Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa,Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;

22. Libanthuke phewa langa paphalo,Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.

23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

24. Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga,Ndi kunena ndi golidi woyengetsa,Ndiwe cikhazikitso canga;

25. Ngati ndinakondwera popeza cuma canga ncacikuru,Ndi dzanja langa lapeza zocuruka;

Werengani mutu wathunthu Yobu 31