Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 30:8-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndiwo ana a opusa, inde ana a anthu opanda dzina;Anawaingitsa kuwacotsa m'dziko.

9. Koma tsopano ndasanduka nyimbo ya oterewo,Nandiyesa nthanthi.

10. Anyansidwa nane, akhala patali ndi ine,Saleka kuthira malobvu pankhope panga.

11. Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza;Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.

12. Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.

13. Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14. Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

15. Anditembenuzira zondiopsa,Auluza ulemu wanga ngati mphepo;Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.

16. Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga;Masiku akuzunza andigwira.

17. Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine,Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.

18. Mwa mphamvu yaikuru ya nthenda yanga cobvala canga cinasandulika,Cindithina ngati pakhosi pa maraya anga.

Werengani mutu wathunthu Yobu 30