Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 30:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakati pa zitsamba alira ngati buru,Pansi pa khwisa asonkhana pamodzi.

8. Ndiwo ana a opusa, inde ana a anthu opanda dzina;Anawaingitsa kuwacotsa m'dziko.

9. Koma tsopano ndasanduka nyimbo ya oterewo,Nandiyesa nthanthi.

10. Anyansidwa nane, akhala patali ndi ine,Saleka kuthira malobvu pankhope panga.

11. Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza;Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.

12. Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.

13. Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14. Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

Werengani mutu wathunthu Yobu 30