20. Ndipfuula kwa Inu, koma simundiyankha;Ndinyamuka, ndipo mungondipenyerera.
21. Mwasandulika kundicitira nkharwe;Ndi mphamvu ya dzanja lanu mundizunza.
22. Mundikweza kumphepo, mundiyendetsa pomwepo;Ndipo mundisungunula mumkuntho.
23. Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa,Ndi ku nyumba yokomanamo amoyo onse.
24. Koma munthu akati agwe, satambasula dzanja lace kodi?Akati aonongeke, sapfuulako kodi?