Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 30:12-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.

13. Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14. Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

15. Anditembenuzira zondiopsa,Auluza ulemu wanga ngati mphepo;Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.

16. Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga;Masiku akuzunza andigwira.

17. Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine,Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.

18. Mwa mphamvu yaikuru ya nthenda yanga cobvala canga cinasandulika,Cindithina ngati pakhosi pa maraya anga.

19. Iye anandiponya m'matope,Ndipo ndafanana ndi pfumbi ndi phulusa.

20. Ndipfuula kwa Inu, koma simundiyankha;Ndinyamuka, ndipo mungondipenyerera.

21. Mwasandulika kundicitira nkharwe;Ndi mphamvu ya dzanja lanu mundizunza.

22. Mundikweza kumphepo, mundiyendetsa pomwepo;Ndipo mundisungunula mumkuntho.

23. Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa,Ndi ku nyumba yokomanamo amoyo onse.

24. Koma munthu akati agwe, satambasula dzanja lace kodi?Akati aonongeke, sapfuulako kodi?

25. Kodi sindinamlirira misozi wakulawa zowawa?Kodi moyo wanga sunacitira cisoni osowa?

26. Muja ndinayembekeza cokoma cinadza coipa,Ndipo polindira kuunika unadza mdima.

Werengani mutu wathunthu Yobu 30