Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 30:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.

13. Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14. Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

15. Anditembenuzira zondiopsa,Auluza ulemu wanga ngati mphepo;Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.

16. Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga;Masiku akuzunza andigwira.

17. Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine,Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.

Werengani mutu wathunthu Yobu 30