Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 3:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.

9. Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;

10. Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga.Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.

11. Ndinalekeranji kufera m'mimba?Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?

12. Anandilandiriranji maondo?Kapena mabere kuti ndiyamwe?

13. Pakuti ndikadagona pansi pomwepo ndi kukhala cete;Ndikanagona tulo; pamenepo ndikadaona popumula;

14. Pamodzi ndi mafumu ndi maphungu a padziko,Akudzimangira m'mabwinja;

15. Kapena pamodzi ndi akalonga eni ace a golidi,Odzaza nyumba zao ndi siliva;

16. Kapena ngati nsenye yobisika ndikadakhala kuli zi;Ngati makanda osaona kuunika.

17. Apo oipa aleka kumabvuta;Ndi apo ofoka mphamvu akhala m'kupumula.

18. Apo a m'kaidi apumula pamodzi,Osamva mau a wofulumiza wao.

19. Ang'ono ndi akulu ali komwe;Ndi kapolo amasuka kwa mbuyace.

20. Amninkhiranji kuunika wobvutika,Ndi moyo kwa iye wakuwawa mtima,

Werengani mutu wathunthu Yobu 3