Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 3:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Litayike tsiku lobadwa ine,Ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.

4. Tsiku lija likhale mdima;Mulungu asalifunse kumwamba,Ndi kuunika kusaliwalire.

5. Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese lao lao;Mtambo ulikhalire;Zonse zodetsa usana bi ziliopse.

6. Usiku uja, mdima weni weni uugwere;Usakondwerere mwa masiku a m'caka;Usalowe m'ciwerengedwe ca miyezi.

7. Ha! usiku uja ukhale cumba;Kuyimbira kokondwera kusalowem'mwemo.

8. Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.

9. Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;

Werengani mutu wathunthu Yobu 3