Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 3:19-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ang'ono ndi akulu ali komwe;Ndi kapolo amasuka kwa mbuyace.

20. Amninkhiranji kuunika wobvutika,Ndi moyo kwa iye wakuwawa mtima,

21. Wakuyembekezera imfa, koma kuli zi,Ndi kuikumba koposa cuma cobisika,

22. Wakusekerera ndi cimwemweNdi kukondwera pakupeza manda?

23. Amuonetseranji kuunika munthu wa njira yobisika,Amene wamtsekera Mulungu?

24. Pakuti ndikati ndidye, kumadza kuusa moyo kwanga;Ndi kudzuma kwanga kumathiridwa ngati madzi.

25. Pakuti cimene ndinaciopa candigwera,Ndi cimene ndacita naco mantha candidzera.

26. Wosakhazikika, ndi wosakhala cete, ndi wosapumula ine,Koma mabvuto anandidzera.

Werengani mutu wathunthu Yobu 3